32 Mulungu ndiye wondizingiza mphamvu m'cuuno,Nakonza njira yanga ikhale yangwiro.
33 Alinganiza mapazi anga ngati a nswala:Nandiimitsa pamsanje panga.
34 Aphunzitsa manja anga agwire nkhondo;Kuti walifuka uta wamkuwa ndi manja anga.
35 Ndipo mwandipatsa cikopa ca cipulumutso canu:Ndipo dzanja lamanja lanu landigwiriziza,Ndipo cifatso canu candikuza ine.
36 Mwandipondetsa patali patali,Sanaterereka mapazi anga.
37 Ndidzalondola adani anga, ndi kuwapeza:Ndipo sindidzabwerera asanathe psiti.
38 Ndidzawapyoza kuti sangakhoze kuuka:Adzagwa pansi pa mapazi anga,