40 Ndipo adani anga mwawalozetsa m'mbuyo kwa ine,Kuti ndipasule ondidawo.
41 Anapfuula, koma panalibewopulumutsa;Ngakhale kwa Yehova, koma sanawabvomereza.
42 Pamenepo ndinawapera ngati pfumbi la kumphepo;Ndinawakhuthula ngati matope a pabwalo.
43 Mwandipulumutsa pa zolimbana nane za anthu;Mwandiika mutu wa amitundu;Mtundu wa anthu sindinaudziwa udzanditumikira.
44 Pakumva m'khutu za ine adzandimvera:Alendo adzandigonjera monyenga.
45 Alendo adzafota,Nadzaturuka monjenjemera m'ngaka mwao.
46 Yehova ngwa moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;Nakwezeke Mulungu wa cipulumutso canga: