43 Mwandipulumutsa pa zolimbana nane za anthu;Mwandiika mutu wa amitundu;Mtundu wa anthu sindinaudziwa udzanditumikira.
44 Pakumva m'khutu za ine adzandimvera:Alendo adzandigonjera monyenga.
45 Alendo adzafota,Nadzaturuka monjenjemera m'ngaka mwao.
46 Yehova ngwa moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;Nakwezeke Mulungu wa cipulumutso canga:
47 Ndiye Mulungu amene andibwe, zerera cilango,Nandigonjetsera mitundu ya anthu.
48 Andipulumutsa kwa adani anga:Inde mundikweza pa iwo akundiukira ine:Mundikwatula kwa munthu waciwawa.
49 Cifukwa cace Yehova ndidzakuyamikani mwa amitundu,Ndipo dzina lanu ndidzaliyimbira.