9 Ndipo Iye anaweramitsa thambo, natsika;Ndipo pansi pa mapazi ace panali mdima bii.
10 Ndipo anaberekeka pa kerubi, nauluka;Nauluka msanga pa mapiko a mphepo,
11 Anaika mdima pobisala pace, hema wace womzinga;Mdima wa madzi, makongwa a kuthambo.
12 Mwa kucezemira kunali pamaso pace makongwa anakanganuka,Matalala ndi makala amoto.
13 Ndipo anagunda m'mwamba Yehova,Ndipo Wam'mwambamwamba anamvetsa liu lace;Matalala ndi makala amoto,
14 Ndipo anatuma mibvi yace nawabalalitsa;Inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.
15 Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi,Nafukuka maziko a dziko lapansi,Mwa kudzudzula kwanu, Yehova,Mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.