3 Koma Inu ndinu woyera,Wakukhala m'malemekezo a Israyeli.
4 Makolo athu anakhulupirira Inu:Anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.
5 Anapfuula kwa Inu, napulumutsidwa:Anakhulupita Inu, ndipo sanacita manyazi.
6 Koma ine ndine nyongolotsi, si munthu ai:Cotonza ca anthu, ndi wonyozedwa ndi anthu.
7 Onse akundipenya andiseka:Akwenzula, apukusa mutu, nati,
8 Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa,Amlanditse tsopano popeza akondwera naye.
9 Pakuti Inu ndinu wondibadwitsa:Wondikhulupiritsa pokhala ine pa bere la mai wanga.