7 Onse akundipenya andiseka:Akwenzula, apukusa mutu, nati,
8 Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa,Amlanditse tsopano popeza akondwera naye.
9 Pakuti Inu ndinu wondibadwitsa:Wondikhulupiritsa pokhala ine pa bere la mai wanga.
10 Cibadwire ine anandisiyira Inu:Kuyambira kwa mai wanga Mulungu wanga ndinu.
11 Musandikhalire kutali; pakuti nsautso iri pafupi:Pakuti palibe mthandizi.
12 Ng'ombe zamphongo zambiri zandizinga:Mphongo zolimba za ku Basana zandizungulira,
13 Andiyasamira m'kamwa mwao,Ngati mkango wozomola ndi wobangula.