9 Pakuti Inu ndinu wondibadwitsa:Wondikhulupiritsa pokhala ine pa bere la mai wanga.
10 Cibadwire ine anandisiyira Inu:Kuyambira kwa mai wanga Mulungu wanga ndinu.
11 Musandikhalire kutali; pakuti nsautso iri pafupi:Pakuti palibe mthandizi.
12 Ng'ombe zamphongo zambiri zandizinga:Mphongo zolimba za ku Basana zandizungulira,
13 Andiyasamira m'kamwa mwao,Ngati mkango wozomola ndi wobangula.
14 Ndathiridwa pansi monga madzi,Ndipo mafupa anga onse anaguluka:Mtima wanga ukunga sera; Wasungunuka m'kati mwa matumbo anga,
15 Mphamvu yanga yauma ngati phale;Ndi lilime langa likangamira ku nsaya zanga;Ndipo mwandifikitsa ku pfumbi la imfa.