1 Pfuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima:Oongoka mtima ayenera kulemekeza.
2 Yamikani Yehova ndi zeze:Myimbireni ndi cisakasa ca zingwe khumi.
3 Mumyimbire Iye Nyimbo yatsopano;Muyimbe mwaluso kumveketsa mau.
4 Pakuti mau a Yehova ali olunjika;Ndi nchito zace zonse zikhulupirika.
5 Iye ndiye wakukonda cilungamo ndi ciweruzo:Dziko lapansi ladzala ndi cifundo ca Yehova.
6 Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova;Ndipo ndi mpweya wa m'kamwa mwace khamu lao lonse.
7 Amaunjika madzi a m'nyanja monga mulu:Amakundika zakudya mosungiramo.