14 M'malo akhalamo Iye, amapenya pansiPa onse akukhala m'dziko lapansi;
15 Iye amene akonza mitima ya iwo onse,Amene azindikira zocita zao zonse.
16 Palibe mfumu yoti gulu lalikuru limpulumutsa:Mphamvu yaikuru siicilanditsa ciphona,
17 Kavalo safikana kupulumuka naye:Cinkana mphamvu yace njaikuru sapulumutsa.
18 Taonani, diso la Yehova liri pa iwo akumuopa Iye,Pa iwo akuyembekeza cifundo cace;
19 Kupulumutsa moyo wao kwa imfa,Ndi kuwasunga ndi moyo m'nyengo ya njala.
20 Moyo wathu walindira Yehova:Iye ndiye thandizo lathu ndi cikopa cathu.