16 Palibe mfumu yoti gulu lalikuru limpulumutsa:Mphamvu yaikuru siicilanditsa ciphona,
17 Kavalo safikana kupulumuka naye:Cinkana mphamvu yace njaikuru sapulumutsa.
18 Taonani, diso la Yehova liri pa iwo akumuopa Iye,Pa iwo akuyembekeza cifundo cace;
19 Kupulumutsa moyo wao kwa imfa,Ndi kuwasunga ndi moyo m'nyengo ya njala.
20 Moyo wathu walindira Yehova:Iye ndiye thandizo lathu ndi cikopa cathu.
21 Pakuti mtima wathu udzakondwera mwa Iye,Cifukwa takhulupirira dzina lace loyera.
22 Yehova, cifundo canu cikhale pa ife,Monga takuyembekezani Inu.