4 Pakuti mau a Yehova ali olunjika;Ndi nchito zace zonse zikhulupirika.
5 Iye ndiye wakukonda cilungamo ndi ciweruzo:Dziko lapansi ladzala ndi cifundo ca Yehova.
6 Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova;Ndipo ndi mpweya wa m'kamwa mwace khamu lao lonse.
7 Amaunjika madzi a m'nyanja monga mulu:Amakundika zakudya mosungiramo.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova:Ponse pali anthu acite mantha cifukwa ca Iye,
9 Pakuti ananena, ndipo cinacitidwa;Analamulira, ndipo cinakhazikika.
10 Yehova aphwanya upo wa amitundu:Asandutsa cabe zolingirira za mitundu ya anthu.