9 Pakuti ananena, ndipo cinacitidwa;Analamulira, ndipo cinakhazikika.
10 Yehova aphwanya upo wa amitundu:Asandutsa cabe zolingirira za mitundu ya anthu.
11 Ciweruzo ca Yehova cikhazikika cikhazikikire,Zolingirira za m'mtima mwace ku mibadwo mibadwo.
12 Wodalitsika mtundu wa anthu umene Yehova ndiye Mulungu wao;Mtundu womwe anausankha ukhale colandira ca iye yekha.
13 Yehova apenyerera m'mwamba; Aona ana onse a anthu.
14 M'malo akhalamo Iye, amapenya pansiPa onse akukhala m'dziko lapansi;
15 Iye amene akonza mitima ya iwo onse,Amene azindikira zocita zao zonse.