3 Bukitsani pamodzi ndine ukuru wa Yehova,Ndipo tikweze dzina lace pamodzi.
4 Ndinafuna Yehova ndipo anandibvomera,Nandlianditsa m'mantha anga Onse.
5 Iwo anayang'ana Iye nasanguruka;Ndipo pankhope pao sipadzacita manyazi,
6 Munthu uyu wozunzika anapfuula, ndipo Yehova anamumva,Nampulumutsa m'masautso ace onse.
7 Mngelo wa Yehova azinga kuwacinjiriza iwo akuopa Iye,Nawalanditsa iwo.
8 Talawani, ndipo onani kuti Yehova ndiye wabwino;Wodala munthuyo wakukhulupirira Iye.
9 Opani Yehova, inu oyera mtima ace;Cifukwa iwo akumuopa Iye sasowa.