17 Ambuye, mudzapenyerabe nthawi yanji?Bwezani moyo wanga kwa zakundiononga zao,Wanga wa wokha kwa misona ya mkango.
18 Ndidzakuyamikanimumsonkhano waukuru:M'cikhamu ca anthu ndidzakulemekezani.
19 Adani anga asandikondwerere ine monyenga;Okwiya nane kopanda cifukwa asanditsinzinire.
20 Pakuti salankhula zamtendere:Koma apangira ciwembu odekha m'dziko.
21 Ndipo andiyasamira m'kamwa mwao;Nati, Hede, Hede, diso lathu lidacipenya.
22 Yehova, mudacipenya; musakhale cete:Ambuye, musakhale kutali ndi ine.
23 Galamukani, ndipo khalani maso kundiweruzira mlandu wanga,Mulungu wanga ndi Ambuye wanga,