1 Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa,Usacite nsanje cifukwa ca ocita cosalungama.
2 Pakuti adzawamweta msanga monga udzu,Ndipo adzafota monga msipu wauwisi.
3 Khulupirira Yehova, ndipo cita cokoma;Khala m'dziko, ndipo tsata coonadi.
4 Udzikondweretsenso mwa Yehova;Ndipo iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.