20 Pakuti oipa adzatayika,Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa:Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.
21 Woipa akongola, wosabweza:Koma wolungama acitira cifundo, napereka.
22 Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.
23 Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;Ndipo akondwera nayo njira yace.
24 Angakhale akagwa, satayikiratu:Pakuti Yehova agwira dzanja lace.
25 Ndinali mwana ndipo ndakalamba:Ndipo sindinapenya wolungama wasiyidwa,Kapena mbumba zace zirinkupempha cakudya.
26 Tsiku lonse acitira cifundo, nakongoletsa;Ndipo mbumba zace zidalitsidwa.