6 Ndipo adzaonetsa cilungamo cako monga kuunika,Ndi kuweruza kwako monga usana.
7 Khala cete mwa Yehova, numlindirire Iye:Usabvutike mtima cifukwa ca iye wolemerera m'njira yace,Cifukwa ca munthu wakucita ciwembu.
8 Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo:Usabvutike mtima ungacite coipa,
9 Pakuti ocita zoipa adzadulidwa:Koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.
10 Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti:Inde, udzayang'anira mbuto yace, nudzapeza palibe.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi;Nadzakondwera nao mtendere wocuruka.
12 Woipa apangira ciwembu wolungama,Namkukutira mano.