4 Inu ndinu mfumu yanga, Mulungu:Lamulirani cipulumutso ca Yakobo.
5 Mwa Inu tidzakankhira pansi otsutsana nafe:M'dzina lanu tidzapondereza akutiukira ife.
6 Pakuti sinditama uta wanga,Ndipo lupanga langa silingandipulumutse.
7 Koma Inu munatipulumutsa kwa iwo akutsutsana nafe,Ndipo akudana nafe, mudawacititsa manyazi.
8 Mwa Mulungu tidzitamanda tsiku lonse,Ndipo dzina lanu tidzaliyamika kosatha.
9 Koma mwatitaya, ndi kutinyazitsa;Ndipo simuturuka nao makamu a nkhondo athu.
10 Mutibwereretsa kuthawa otisautsa:Ndipo akudana nafe adzifunkhira okha.