17 Pakuti pomwalira iye sadzamuka nako kanthu kali konse;Ulemu wace sutsika naye kumtsata m'mbuyo.
18 Angakhale anadalitsa moyo wace pokhala ndi moyo,Ndipo anthu akulemekeza iwe, podzicitira wekha zokoma,
19 Adzamuka ku mbadwo wa makolo ace;Sadzaona kuunika nthawi zonse.
20 Munthu waulemu, koma wosadziwitsa,Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.