4 Ndidzachera khutu kufanizo:Ndidzafotokozera cophiphiritsa canga poyimbira.
5 Ndidzaoperanji masiku oipa,Pondizinga amphulupulu onditsata kucidendene?
6 Iwo akutama kulemera kwao;Nadzitamandira pa kucuruka kwa cuma cao;
7 Kuombola mbale sangadzamuombole,Kapena kumperekera dipo kwa Mulungu:
8 (Popeza ciombolo ca moyo wao nca mtengo wace wapatali,Ndipo cilekeke nthawi zonse)
9 Kuti akhale ndi moyo osafa,Osaona cibvundi.
10 Pakuti aona anzeru amafa,Monga aonongekera wopusa, wodyerera momwemo,Nasiyira ena cuma cao.