8 (Popeza ciombolo ca moyo wao nca mtengo wace wapatali,Ndipo cilekeke nthawi zonse)
9 Kuti akhale ndi moyo osafa,Osaona cibvundi.
10 Pakuti aona anzeru amafa,Monga aonongekera wopusa, wodyerera momwemo,Nasiyira ena cuma cao.
11 Mumtima mwao ayesa kuti nyumba zao zikhala cikhalire,Ndi mokhala iwo ku mibadwo mibadwo;Achapo dzina lao padziko pao.
12 Koma munthu wa ulemu wace sakhalitsa:Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.
13 Njira yao yino ndiyo kupusa kwao:Koma akudza m'mbuyo abvomereza mau ao.
14 Aikidwa m'manda ngati nkhosa;Mbusa wao ndi imfa:Ndipo m'mawa mwace oongoka mtima adzakhala mafumu ao;Ndipo maonekedwe ao adzanyekera kumanda, kuti pokhala pace padzasowa.