3 Cifukwa ndazindikira macimo anga;Ndipo coipa canga ciri pamaso panga cikhalire:
4 Pa Inu, Inu nokha, ndinacimwa,Ndipo ndinacicita coipaco pamaso panu:Kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu,Mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.
5 Onani, ndinabadwa m'mphulupulu:Ndipo mai wanga anandilandira m'zoipa.
6 Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m'malo a m'katimo;Ndipo m'malo a m'tseri mudzandidziwitsa nzeru.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera;Munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbu woposa matalala.
8 Mundimvetse cimwemwe ndi kusekera:Kuti mafupawo munawatyola akondwere.
9 Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga,Ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.