1 Kodi muli cete ndithu poyenera inu kunena zolungama?Muweruza ana a anthu molunjika kodi?
2 Inde, mumtima mucita zosalungama;Pa dziko lapansi mugawira anthu ciwawa ca m'manja mwanu.
3 Oipa acita cilendo cibadwire:Asokera kuyambira kubadwa kwao, nanena bodza.
4 Ululu wao ukunga wa njoka;Akunga mphiri yogontha m'khutu, itseka m'khutu mwace.