4 Ululu wao ukunga wa njoka;Akunga mphiri yogontha m'khutu, itseka m'khutu mwace.
5 Imene simvera liu la oitana,Akucita matsenga mocenieratu,
6 Tyolani mano ao m'kamwa mwao, Mulungu:Zulani zitsakano za misona ya mkango, Yehova.
7 Apitetu ngati madzi oyenda;Popiringidza mibvi yace ikhale yodukaduka.
8 Apite ngati nkhono yosungunuka;Asaone dzuwa monga mtayo,
9 Miphika yanu isanagwire moto waminga,Adzaiuluza, yaiwisi ndi yoyaka.
10 Wolungama adzakondwera pakuona kubwezera cilango:Adzasamba mapazi ace m'mwazi wa woipa.