1 Yehova Mulungu wanga, ndakhulupirira Inu:Mundipulumutse kwa onse akundilonda, nimundilanditse;
2 Kuti angamwetule moyo wanga ngati mkango,Ndi kuukadzula, wopanda wina wondilanditsa.
3 Yehova Mulungu wanga, ngati ndacita ici;Ngati m'manja anga muli cosalungama;
4 Ngati ndambwezera coipa iye woyanjana ndine;(Inde, ndamlanditsa wondisautsa kopanda cifukwa);