9 Musanditaye mu ukalamba wanga;Musandisiye, pakutha mphamvu yanga.
10 Pakuti adani anga alankhula za ine;Ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,
11 Ndi kuti, Wamsiya Mulungu:Mlondoleni, mgwireni; popeza palibe wompulumutsa,
12 Musandikhalire kutali, Mulungu;Fulumirani kundithandiza, Mulungu;
13 Adani a moyo wanga acite manyazi, nathawe;Cotonza ndi cimpepulo zikute ondifunira coipa,
14 Koma ine ndidzayembekeza kosaleka,Ndipo ndidzaonjeza kukulemekezani.
15 Pakamwa panga padzafotokozera cilungamo canu,Ndi cipulumutso canu tsiku lonse;Pakuti sindidziwa mawerengedwe ace.