14 Popeza andisautsa tsiku lonse,Nandilanga mamawa monse,
15 Ndikadati, Ndidzafotokozera cotere,Taonani, ndikadacita cosakhulupirika ndi mbadwo wa ana ako.
16 Pamene ndinayesa kudziwitsa ici,Ndinabvutika naco;
17 Mpaka ndinalowa m'zoyera za Mulungu,Ndi kulingalira citsiriziro cao.
18 Indedi muwaika poterera:Muwagwetsa kuti muwaononge.
19 Ha! m'kamphindi ayesedwa bwinja;Athedwa konse ndi zoopsya.
20 Monga anthu atauka, apepula loto;Momwemo, Inu Ambuye, pakuuka mudzapeputsa cithunzithunzi cao.