18 Indedi muwaika poterera:Muwagwetsa kuti muwaononge.
19 Ha! m'kamphindi ayesedwa bwinja;Athedwa konse ndi zoopsya.
20 Monga anthu atauka, apepula loto;Momwemo, Inu Ambuye, pakuuka mudzapeputsa cithunzithunzi cao.
21 Pakuti mtima wanga udawawa,Ndipo ndinalaswa m'imso zanga;
22 Ndinali wam'thengo, wosadziwa kanthu;Ndinali ngati nyama pamaso panu.
23 Koma ndikhala ndi Inu cikhalire:Mwandigwira dzanja langa la manja.
24 Mudzanditsogolera ndi uphungu wanu,Ndipo mutatero, mudzandilandira m'ulemerero,