2 Koma ine, ndikadagwa; Mapazi anga akadaterereka,
3 Pakuti ndinacitira nsanje odzitamandira,Pakuona mtendere wa oipa,
4 Pakuti palibe zomangira pakufa iwo:Ndi mphamvu yao niolimba,
5 Sabvutika monga anthu ena;Sasautsika monga anthu ena.
6 Cifukwa cace kudzikuza kunga unyolo pakhosi pao;Acibvala ciwawa ngati malaya.
7 Kunenepa kwao kutuzulitsa maso ao:Malingaliro a mitima yao asefukira.
8 Acita zaphwete nalankhula moipa za kusautsa:Alankhula modzitama.