25 Ndiri ndi yani Kumwamba, koma Inu?Ndipo Pa dziko lapansi palibe wina wondikonda koma Inu.
26 Likatha thupi langa ndi mtima wanga:Mulungu ndiye thanthwe la mtima wanga, ndi colandira canga cosatha.
27 Pakuti, taonani, iwo okhala patali ndi Inu adzaonongeka;Muononga onse akupembedza kwina, kosiyana ndi Inu.
28 Koma ine, kundikomera kuyandikiza kwa Mulungu:Ndimuyesa Ambuye Yehova pathawirapo ine,Kuti ndifotokozere nchito zanu zonse,