13 Mudagawa nyanja ndi mphamvu yanu;Mudaswa mitu ya zoopsa za m'madzi.
14 Mudaphwanya mitu ya livyatanu;Mudampereka akhale cakudya ca iwo a m'cipululu.
15 Mudagawa kasupe ndi mtsinje;Mudaphwetsa mitsinje yaikuru.
16 Usana ndi wanu, usikunso ndi wanu:Munakonza kuunika ndi dzuwa.
17 Munaika malekezero onse a dziko lapansi;Munalenga dzinja ndi malimwe.
18 Mukumbukile ici, Yehova, mdaniyo anatonza,Ndipo anthu opusa ananyoza dzina lanu.
19 Musapereke moyo wa njiwa yanu kwa cirombo;Musamaiwala moyo wa ozunzika anu nthawi yonse.