17 Munaika malekezero onse a dziko lapansi;Munalenga dzinja ndi malimwe.
18 Mukumbukile ici, Yehova, mdaniyo anatonza,Ndipo anthu opusa ananyoza dzina lanu.
19 Musapereke moyo wa njiwa yanu kwa cirombo;Musamaiwala moyo wa ozunzika anu nthawi yonse.
20 Samalirani cipanganoco;Pakuti malo amdima a m'dziko adzala ndi zokhalamo ciwawa.
21 Okhalira mphanthi asabwere nao manyazi;Wozunzika ndi waumphawi alemekeze dzina lanu.
22 Nyamukani, Mulungu, mudzinenere mlandu nokha;Kumbukilani momwe akutonzani wopusa tsiku lonse.
23 Musaiwale mau a iwo otsutsana ndi Inu;Kusokosera kwa iwo akuukirani Inu kumakweca kosaleka.