19 Musapereke moyo wa njiwa yanu kwa cirombo;Musamaiwala moyo wa ozunzika anu nthawi yonse.
20 Samalirani cipanganoco;Pakuti malo amdima a m'dziko adzala ndi zokhalamo ciwawa.
21 Okhalira mphanthi asabwere nao manyazi;Wozunzika ndi waumphawi alemekeze dzina lanu.
22 Nyamukani, Mulungu, mudzinenere mlandu nokha;Kumbukilani momwe akutonzani wopusa tsiku lonse.
23 Musaiwale mau a iwo otsutsana ndi Inu;Kusokosera kwa iwo akuukirani Inu kumakweca kosaleka.