3 Nyamulani mapazi anu kukapenya mapasukidwe osatha,Zoipa zonse adazicita mdani m'malo opatulika.
4 Otsutsana ndi Inu abangula pakati pa msonkhano wanu;Aika mbendera zao zikhale zizindikilo.
5 Anaoneka ngati osamula nkhwangwa kunkhalango.
6 Ndipo tsopano aphwanya zosemeka zace zonseNdi nkhwangwa ndi nyundo,
7 Anatentha malo anu opatulika;Anaipsa ndi kugwetsa pansi mokhalamo dzina lanu.
8 Ananena mumtima mwao, Tiwapasule pamodzi;Anatentha zosonkhaniramo za Mulungu zonse, m'dzikomo.
9 Sitiziona zizindikilo zathu;Palibenso mneneri;Ndipo mwa ife palibe wina wakudziwa mpaka liti.