4 Otsutsana ndi Inu abangula pakati pa msonkhano wanu;Aika mbendera zao zikhale zizindikilo.
5 Anaoneka ngati osamula nkhwangwa kunkhalango.
6 Ndipo tsopano aphwanya zosemeka zace zonseNdi nkhwangwa ndi nyundo,
7 Anatentha malo anu opatulika;Anaipsa ndi kugwetsa pansi mokhalamo dzina lanu.
8 Ananena mumtima mwao, Tiwapasule pamodzi;Anatentha zosonkhaniramo za Mulungu zonse, m'dzikomo.
9 Sitiziona zizindikilo zathu;Palibenso mneneri;Ndipo mwa ife palibe wina wakudziwa mpaka liti.
10 Wotsutsanayo adzatonza kufikira liti, Mulungu?Kodi mdani adzanyoza dzina lanu nthawi yonse?