3 Ndikumbukila Mulungu ndipo ndibvutika;Ndilingalira ndipo mzimu wanga ukomoka.
4 Mundikhalitsa maso;Ndigwidwa mtima wosanena kanthu.
5 Ndinaganizira masiku akale, zaka zakalekale.
6 Ndikumbukila Nyimbo yanga, usiku;Ndilingalira mumtima mwanga;Mzimu wanga unasanthula.
7 Kodi Mulungu adzataya nthawi yonse?Osabwerezanso kukondwera nafe.
8 Cifundo cace calekeka konse konse kodi?Lonjezano lace lidatha kodi ku mibadwo yonse?
9 Kodi Mulungu waiwala kucita cifundo?Watsekereza kodi nsoni zokoma zace mumkwiyo?