10 Sanasunga cipangano ca Mulungu,Nakana kuyenda m'cilamulo cace.
11 Ndipo anaiwala zocita Iye,Ndi zodabwiza zace zimene anawaonetsa.
12 Anacita codabwiza pamaso pa makolo ao,M'dziko la Aigupto ku cidikha ca Zoanu.
13 Anagawa nyanja nawapititsapo;Naimitsa madziwo ngati khoma.
14 Ndipo msana anawatsogolera ndi mtamboNdi usiku wonse ndi kuunika kwa moto.
15 Anang'alula thanthwe m'cipululu,Ndipo anawamwetsa kocuruka monga m'madzi ozama.
16 Anaturukitsa mitsinje m'thanthwe,Inde anatsikitsa madzi ngati mitsinje.