20 Taonani, anapanda thanthwe, ndi madzi anayendakoNdi mitsinje inasefuka;Kodi adzakhozanso kupatsa mkate?Kodi adzafunira anthu ace nyama?
21 Cifukwa cace Yehova anamva, nakwiya;Ndipo anayatsa moto pa Yakobo,Ndiponso mkwiyo unakwera pa Israyeli;
22 Popeza sanakhulupirira Mulungu,Osatama cipulumutso cace.
23 Koma analamulira mitambo iri m'mwamba,Natsegula m'makomo a kumwamba.
24 Ndipo anawabvumbitsira mana, adye,Nawapatsa tirigu wa kumwamba.
25 Yense anadya mkate wa omveka:Anawatumizira cakudya cofikira,
26 Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa:Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.