25 Yense anadya mkate wa omveka:Anawatumizira cakudya cofikira,
26 Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa:Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.
27 Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:
28 Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.
29 Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.
30 Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,
31 Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,Ndipo anapha mwa onenepa ao,Nagwetsa osankhika a Israyeli.