27 Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:
28 Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.
29 Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.
30 Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,
31 Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,Ndipo anapha mwa onenepa ao,Nagwetsa osankhika a Israyeli.
32 Cingakhale ici conse anacimwanso,Osabvomereza zodabwiza zace.
33 Potero anathera masiku ao ndi zopanda pace,Ndi zaka zao mwa mantha.