31 Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,Ndipo anapha mwa onenepa ao,Nagwetsa osankhika a Israyeli.
32 Cingakhale ici conse anacimwanso,Osabvomereza zodabwiza zace.
33 Potero anathera masiku ao ndi zopanda pace,Ndi zaka zao mwa mantha.
34 Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;Nabwerera, nafunitsitsa Mulungu,
35 Ndipo anakumbukila kuti Mulungu ndiye thanthwe lao,Ndi Mulungu Wam'mwambamwamba Mombolo wao.
36 Koma anamsyasyalika pakamwa pao,Namnamiza ndi lilime lao.
37 Popeza mtima wao sunakonzekera Iye,Ndipo sanakhazikika m'cipangano cace.