4 Sitidzazibisira ana ao,Koma kufotokozera mbadwo ukudzawo zolemekeza za Yehova,Ndi mphamvu yace, ndi zodabwiza zace zimene anazicita.
5 Anakhazika mboni mwa Yakobo,Naika cilamulo mwa Israyeli,Ndizo analamulira atate athu,Akazidziwitse ana ao;
6 Kuti mbadwo ukudzawo udziwe, ndiwo ana amene akadzabadwa;Amene adzaimirira nadzafotokozera ana ao:
7 Ndi kuti ciyembekezo cao cikhale kwa Mulungu,Osaiwala zocita Mulungu,Koma kusunga malamulo ace ndiko.
8 Ndi kuti asange makolo ao,Ndiwo mbadwo woukirana ndi wopikisana ndi Mulungu;Mbadwo wosakonza mtima wao,Ndi mzimu wao sunakhazikika ndi Mulungu.
9 Ana a Efraimu okhala nazo zida, oponya nao mauta,Anabwerera m'mbuyo tsiku la nkhondo.
10 Sanasunga cipangano ca Mulungu,Nakana kuyenda m'cilamulo cace.