50 Analambulira mkwiyo wace njira;Sanalekerera moyo wao usafe,Koma anapereka moyo wao kumliri;
51 Ndipo anapha ana oyamba onse a mu Aigupto,Ndiwo oyamba a mphamvu yao m'mahema a Hamu:
52 Koma anaturutsa anthu ace ngati nkhosa,Nawatsogoza ngati gulu la zoweta m'cipululu.
53 Ndipo anawatsogolera mokhulupirika,Kotero kuti sanaopa;Koma nyanja inamiza adani ao.
54 Ndipo anawafikitsa ku malire a malo ace oyera,Ku phiri ili, dzanja lamanja lace lidaligula.
55 Ndipo anapitikitsa amitundu pamaso pao,Nawagawira colowa cao, ndi muyeso,Nakhalitsa mafuko a Israyeli m'mahema mwao.
56 Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam'mwambamwamba,Osasunga mboni zace;