53 Ndipo anawatsogolera mokhulupirika,Kotero kuti sanaopa;Koma nyanja inamiza adani ao.
54 Ndipo anawafikitsa ku malire a malo ace oyera,Ku phiri ili, dzanja lamanja lace lidaligula.
55 Ndipo anapitikitsa amitundu pamaso pao,Nawagawira colowa cao, ndi muyeso,Nakhalitsa mafuko a Israyeli m'mahema mwao.
56 Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam'mwambamwamba,Osasunga mboni zace;
57 Koma anabwerera m'mbuyo, nacita zosakhulupirika monga makolo ao:Anapatuka ngati uta wolenda,
58 Ndipo anautsa mtima wace ndi malo amsanje ao,Namcititsa nsanje ndi mafano osema.
59 Pakumva ici Mulungu, anakwiya, Nanyozatu Israyeli;