61 Napereka mphamvu yace m'ukapolo,Ndi ulemerero wace m'dzanja la msautsi.
62 Naperekanso anthu ace kwa lupanga;Nakwiya naco colandira cace.
63 Moto unapsereza anyamata ao;Ndi anamwali ao sanalemekezeka.
64 Ansembe ao anagwa ndi lupanga;Ndipo amasiye ao sanacita maliro.
65 Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo;Ngati ciphona cakucita nthungululu ndi vinyo.
66 Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo;Nawapereka akhale otonzeka kosatha.
67 Tero anakana hema wa Yosefe;Ndipo sanasankha pfuko la Efraimu;