64 Ansembe ao anagwa ndi lupanga;Ndipo amasiye ao sanacita maliro.
65 Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo;Ngati ciphona cakucita nthungululu ndi vinyo.
66 Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo;Nawapereka akhale otonzeka kosatha.
67 Tero anakana hema wa Yosefe;Ndipo sanasankha pfuko la Efraimu;
68 Koma anasankha pfuko la Yuda,Phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 Ndipo anamanga malo oyera ace ngati kaphiri,Monga dziko lapansi limene analikhazikitsa kosatha.
70 Ndipo anasankha Davide mtumiki wace,Namtenga ku makola a nkhosa: