13 Nguruwe zocokera kuthengo ziukumba,Ndi nyama za kucidikha ziudya,
14 Bwererani, tikupemphani, Mulungu wa makamu;Suzumirani muli m'mwamba, nimupenye, ndi kuzonda mpesa uwu,
15 Ndi tsinde limene dzanja lanu lamanja linaokaeNdi mphanda munadzilimbikitsira.
16 Unapserera ndi moto, unadulidwa;Aonongeka pa kudzudzula kwa nkhope yanu.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu wa pa dzanja lamanja lanu;Pa mwana wa munthu amene munadzilimbikitsira.
18 Potero sitidzabwerera m'mbuyo kukusiyani;Titsitsimutseni, ndipo tidzaitanira dzina lanu.
19 Mutibweze, Yehova Mulungu wa makamu;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.