2 Utsani camuna canu pamaso pa Efraimu ndi Benjamini ndi Manase,Ndipo mutidzere kutipulumutsa.
3 Mutibweze, Mulungu;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.
4 Yehova, Mulungu wa makamu,Mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?
5 Munawadyetsa mkate wa misozi,Ndipo munawamwetsa misozi yambiri.
6 Mutiika kuti atilimbirane anzathu;Ndipo adani athu atiseka mwa iwo okha,
7 Mulungu wa makamu, mutibweze;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.
8 Mudatenga mpesa kucokera ku Aigupto:Munapitikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.