5 Munawadyetsa mkate wa misozi,Ndipo munawamwetsa misozi yambiri.
6 Mutiika kuti atilimbirane anzathu;Ndipo adani athu atiseka mwa iwo okha,
7 Mulungu wa makamu, mutibweze;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.
8 Mudatenga mpesa kucokera ku Aigupto:Munapitikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.
9 Mudasoseratu pookapo,Idagwiritsa mizu yace, ndipo unadzaza dziko.
10 Mthunzi wace unaphimba mapiri,Ndi nthambi zace zikunga mikungudza ya Mulungu.
11 Unatambalitsa mphanda zace mpaka kunyanja,Ndi mitsitsi yace kufikira ku Mtsinje.