8 Asuri anaphatikana nao;Anakhala dzanja la ana a Loti,
9 Muwacitire monga munacitira Midyani;Ndi Sisera, ndi Jabini ku mtsinje wa Kisoni:
10 Amene anaonongeka ku Endoro;Anakhala ngati ndowe ya kumunda.
11 Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;Mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna:
12 Amene anati, TilandeMalo okhalamo Mulungu, akhale athu.
13 Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;Ngati ziputu zomka ndi mphepo.
14 Monga moto upsereza nkhalango,Ndi monga lawi liyatsa mapiri;